"N'chifukwa chiyani Mulungu sakuyankha mapemphero anga?"
Kodi munayamba mwamvapo kuti Mulungu sayankha pemphero nthawi zonse? Kodi munayamba mwakhalapo ndi tsiku limene zinthu zikulakwika ndipo mumapeza kuti mukufuula kwa Mulungu, koma palibe chimene chimasintha? N'chifukwa chiyani Mulungu sakuyankha mapemphero anu?
"Tikudziwa kuti zinthu zonse zimagwira ntchito limodzi kuti anthu amene amakonda Mulungu akhale abwino - amene wawaitana mogwirizana ndi dongosolo lake." Aroma 8:28 .
Ngati mumakhulupirira kuti zinthu zonse zimagwirira ntchito pamodzi kaamba ka zabwino, kodi simukuganiza kuti Mulungu akungoyankha mapemphero anu m'njira yosiyana ndi imene mumayembekezera?
Simungathe kuthawa mayesero anu
Tangoganizani kuti mukugwira ndi kasitomala wovuta kuntchito. Iye mwina akufika pokalipa mokuwa pa inu ndipo mkati mwanu kumaamva mkwiyo ukukulirakulirakwambiri.
Atachoka, mumapemphera kuti kasitomala ameneyu asabwerenso, chifukwa kwenikweni simungathe kupirira kukalipidwanso kachiwiri. Kapena mwina mukuona kuti kukwiya sikunali mmene muyenera kuchitira monga Mkristu. Mumapemphera kuti, "O, chonde musalole kuti kasitomala ameneyo abwerenso, sindikufunanso kukwiya kwambiri kachiwiri." Koma kenako tsiku lotsatira kasitomala yemweyo wabweranso ndipo akukalipanso mokuwa! Kodi mukuganiza kuti Mulungu sanamve pemphero lanu?
"Anzanga okondedwa, musadabwe ndi mayeso opweteka amene mukuvutika nawo, ngati kuti chinachake chachilendo chikukuchitikirani. M'malomwake khalani okondwa kuti mukugawana naye mavuto a Khristu, kuti mukhale odzaza ndi chimwemwe pamene ulemerero wake wavumbulutsidwa." 1 Petro 4:12-13.
N'chifukwa chiyani mumapemphera kuti mayesero achoke? Simungathe kudutsa moyo wanu wonse popanda kukumana ndi munthu amene amakukwiyitsani. Anthu oterowo ali paliponse! Mulungu amakulolani kukumana ndi anthu amenewa kuti mukhale ndi mwayi wogonjetsa mkwiyo wanu ndi kukhala wachikondi ndi woleza mtima.
Wangwiro ndi wathunthu, osasowa kanthu
"Abale ndi alongo anga, mukakhala ndi mavuto osiyanasiyana, muyenera kukhala odzaza ndi chimwemwe, chifukwa mukudziwa kuti mavuto amenewa amayesa chikhulupiriro chanu, ndipo zimenezi zidzakupatsani kuleza mtima. Lolani kuleza mtima kwanu kudzisonyeza bwino lomwe m'zimene mumachita. Mukatero mudzakhala wangwiro ndi wathunthu ndipo mudzakhala ndi zonse zimene mukufuna." Yakobo 1:2-4 .
Kodi imeneyi si njira yabwino kwambiri? Kukhala wangwiro ndi wathunthu, ndi kukhala ndi zonse zomwe mukufuna?
Indedi ! Koma Mulungu anapanga malamulo, ndipo ngati tiwatsatira, ndiye kuti tidzafika kumeneko. Mulungu sadzapanga mkwiyo wanu kutha mwa dzidzidzi tsiku limodzi. Iye akufuna kuona ngati mukufuna kuchita chifuniro Chake ndi kumvera Iye. "Chifuniro chanu chichitike padziko lapansi monga mmene chilili kumwamba." —Mateyu 6:10.
M'malo mofunsa chifukwa chake Mulungu sakukumvetserani, mwina muyenera kufunsa chifukwa chomwe inu simukumvera Mulungu! Ngati mukufunadi kuchita chifuniro cha Mulungu, Iye adzayankha pemphero lanu la kuleza mtima ndi mayeserooyenera amene mungaphunzire kuleza mtima. Ngati mukuona kuti Mulungu sakumva mapemphero anu, dzifunseni ngati mwanenadi kuti "Chifuniro Chanu chichitike" pa chilichonse.
Musapemphere kwa Mulungu kuti achotse mayesero ndi nyengo zovuta; pempherani kwa Iye kuti akupatseni mphamvu kuti mugwiritse ntchito mayesero amenewo kuti mukhale ngati Yesu! Pamenepo Iye adzakhala wofunitsitsa kuyankha mapemphero anu! Pamenepo simudzakhalanso ndi tsiku lina lopanda chiyembekezo!