Popanda chinyengo kapena chiphamaso!
“Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anat kwa iye, ‘Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo!’ Natanieli anafunsa kuti, ‘Kodi mwandidziwa bwanji?’ Yesu anayankha kuti, ‘Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pa mtengo wa mkuyu Filipo asanakuyitane.’” Yohane 1:47-48.
Posachedwapa Yesu akubweranso, ndipo Aisraeli onse owona, auzimu, amene mwa iwo mulibe chinyengo kapena bodza, adzakwatulidwa.
Yesu anali womasulidwa kotheratu ku mitundu yonse ya bodza ndi chiphamaso. Nsembe Yake inali ya mtima wodzikhuthula ndi oona, ndipo anapereka magazi Ake ngati dipo. Koma kulikonse kumene ankapita, ankakumana ndi chinyengo ndi chiphamaso chachipembedzo. Iwo ankalemekeza Mulungu ndi milomo yawo, koma mitima yawo inali kutali ndi Iye.
“Nthawi yomweyo, anthu miyandamiyanda atasonkhana, ndi kumapondanapondana, Yesu anayamba kuyankhula poyamba kwa ophunzira ake, nati, ‘Chenjerani ndi yisiti wa Afarisi, amene ndi chinyengo.’” Luka 12:1.
Apa titha kuona mmene Yesu ankaonera chiphamaso mwachidwi. Anadana nacho! Choncho titha kumvetsa chifukwa chake Yesu anasangalala kwambiri pamene anapeza Natanieli. Yesu sanangomupatsa umboni wapamwamba chabe. Anamuyang’anitsitsa pamene anamuona pansi pa mtengo wa mkuyu.
Otseguka ndi oona mtima, ndi miyoyo yawo ili m’kuunika
Yesu angapereke umboni womwewu kwa Aisraeli onse auzimu—awo amene ali mbali ya mkwatibwi Wake. Kodi anganene zimenezi za inu ndi ine pamene tikugwira ntchito zathu za tsiku ndi tsiku? “Taonani, Mwisraeli ndithu, mwa iye mulibe chinyengo!” Ngati sichoncho, ndiye kuti tiyenera kuonetsetsa kuti Iye athe kunena za ife zimenezi posachedwa, kuti tiumbidwe kwathunthu ndi kukhala okonzeka zakubwera Kwake.
Chofunika kuti munthu alowe m’sukulu ya ophunzira ya Yesu ndi kusiya zonse, ndi kutaya chinyengo chonse, chiphamaso chonse, ndi zoipa zonse (1 Petro 2:1; Yakobo 1:21).
Ndi zabwino kwambiri kukhala ndi ophunzira oona otere, podziwa kuti sitidzakumana ndi choipa chilichonse chochokera kwa iwo. Sakhala ndi zolinga zobisika. Iwo ndi omasuka komanso oona mtima; miyoyo yawo ili m’kuunika. Amaganiza, amalankhula, ndi kuchita zabwino. Sitikumana ndi china chilichonse chochokera kwa iwo. Tikadatha kuyang’ana m’mitima yawo, tikanapeza ubwino wochuluka kuposa umene tingaone kunja. Uwu ndi ubale weniweni ndi woona mtima m’thupi la Khristu. Umakhalabe wolimba masiku abwino ndi oipa pano padziko lapansi, ndi kwa muyaya.
Lidzakhala tsiku lalikulu pamene Yesu adzabweranso kudzatenga “ophunzira” ake amene anali ofunitsitsa kuphunzira, ndi amene Iye mwini wawaphunzitsa mokwanira, kuti akhale chitamando ndi ulemerero wake wamuyaya. Iwo adzakhala miyala yamuyaya mu Yerusalemu Watsopano, ndipo mitundu ya anthu idzayenda m’kuwala ndi ulemerero wake (Chivumbulutso 21). Ulemerero umenewu ndi weniweni kotheratu.
Sungani mtima wanu kukhala woyera
Uthenga wabwino ndi mphamvu yeniyeni yotipulumutsa ku chinyengo chilichonse ndi chiphamaso. Petro analalikira uthenga wabwino, ndipo mitima ya Amitundu inayeretsedwa ndi chikhulupiriro Machitidwe a Atumwi15:9. “Odala ndi amene ali oyera mtima, chifukwa adzaona Mulungu.” Mateyu 5:8. Koma kusunga mitima yathu yoyera sikungochitika kokha. “Ndipotu mtima wako udziwuyang'anira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.” Miyambo 4:23.
Mayesero amabwera ngati maganizo oipa ndi odetsedwa ochokera m’thupi langa ndipo amafuna kupeza malo mumtima mwanga. Apa ndi pamene ndiyenera kumenya nkhondo m’chikhulupiriro kuti mtima wanga ukhale woyera. Si uchimo kuyesedwa, koma ngati nditsegula mtima wanga ku maganizo oipa ndi odetsedwa, pamenepo ndidzakhala woipa ndi wodetsedwa. Sitiyenera kugonjera mdierekezi. Tiyenera kumukaniza, pakukhala okhazikika m’chikhulupiriro. Tiyenera kuletsa mivi yonse yoyaka moto ya woipayo ndi chishango cha chikhulupiriro (Aefeso 6:16).
Kudzera mu chikhulupiriro mwa Khristu, n’zothekadi kusunga mitima yathu yoyera, yopanda kunyenga kapena chiphamaso, ngakhale m’masiku otsiriza oipa ano pamene anthu ali ndi maonekedwe a chipembedzo koma amakana mphamvu yake (2 Timoteyo 3:5).
Mzimu wokhazikika
“Zoonadi Inu mumafuna choonadi mu ziwalo zam'kati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru m'kati mwanga mwenimweni.” Salmo 51:6. Ngati Mulungu alibe malo m’kati mwenimweni ndi mozama kwambiri mwa mtima wanga, Iye sangandipatse chimene amachikonda kwambiri—nzeru zake, zimene koposa zonse ndi zoyera. “Mulenge mkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.” Salmo 51:10.
Mzimu uwu si wogwedezeka, wokayikakayika kapena wosinthasintha, koma ndi wokhazikika ndi wodalirika, mzimu umene Mulungu ndi anthu angadalire pa zonse zolemekezeka, zabwino ndi zoona. Uwu ndi mtundu wa abale amene Yesu ali nawo, amene Iye adzasangalala nawo kwamuyaya mu ulemerero waukulu kwambiri. Ndipo Yesu ndiye woyamba kubadwa pakati pa abale oterewa (Aroma 8:29).