Kusinthika pamaso panga

Kusinthika pamaso panga

Ndikudziwa kuti n’zotheka kusintha, chifukwa ndaziona mwa amayi anga.

9/19/20264 mphindi

Ndi Moyo wa Chikirisitu Wochitachita

Kusinthika pamaso panga

Ndine mwana wachisanu ndi chiwiri m’banja la ana khumi. Nyumba yathu nthawi zonse inali yaphokoso komanso yotanganidwa pamene tinkakula. Tinkachita phokoso ndipo sitinkamvera kwambiri kapena kukhala osavuta kusamalira. Koma pamene tinkakula, tinkatha kuzindikira kuti chinachake chikuchitika m’moyo wa amayi anga. Panali kusintha kwenikweni komwe kunkachitika mwa iwo.

Mwachibadwa, amayi anga ankatha kukwiya mosavuta. Ngakhale kuti ankayesetsa kukhala mayi wabwino kwambiri mmene akanathera—ndipo anali mayi wabwino kwambiri—ankakwiya ndi kukhumudwa mosavuta.

Kaonedwe katsopano ka nyengozo

Koma patapita nthawi tinayamba kuzindikira kuti zinthu zimene zinkawakhumudwitsa kale sizinkaonekanso kuti zili ndi zotsatira zimenezo. Samadandaulanso kuti zinthu sizinali zachilungamo, ndipo sitinkamvanso kuti chilichonse chinali cholemetsa kwambiri kwa iwo. Posachedwapa, pokambirana nawo, ndinapeza yankho la kusintha kumeneku kumene tinaona.

“Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga. Tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo!” Salmo 118:24.

 Amayi anga anandiuza kuti anaganiza zokhulupirira vesi limeneli, ndipo analigwiritsitsa. Kaya chachitika n’chiyani pa tsikulo, ankabwereza vesi limeneli mumtima mwawo kuti, “Lero ndi tsiku limene Yehova wapanga; ndidzakondwera ndi kusangalala lero.” Ndipo zimenezi zimatanthauzanso kuti ngakhale pamene zinthu zinkaoneka ngati zikutsutsana nawo, lero linalinso tsiku limene Yehova wapanga, ndipo zochitika zimenezi zinasankhidwa mosamala ndi Mulungu kwa iwo.

Kuchokera munyengo zimenezi ndi pamene anazindikira tchimo lomwe linali mu umunthu wawo—kusaleza mtima, kukwiya—zimene zimawalepheretsa pa chikhumbo chawo chokhala nthawi zonse woleza mtima, wachikondi, ndi wofatsa. Koma pozindikira malire awo zinatanthauza kuti akanatha kuchitapo kanthu, ndipo m’Mawu a Mulungu anapeza thandizo lochitira zimenezi. Anaphunzira kuzilandira monga Yakobo akutiuza kuti tichite:

 “Abale, muchiyese ngati chimwemwe chenicheni nthawi zonse pamene mukukumana ndi mayesero amitundumitundu.  Inu mukudziwa kuti kuyesedwa kwa chikhulupiriro chanu kumabweretsa chipiliro.  Chipiriro chiyenera kugwira ntchito yake kuti mukhale okhwima ndi angwiro, osasowa kanthu kalikonse.” Yakobo 1:2-4.

Anaphunzira kukhala wokondwa munyengo monga mmene zinalili. Kunali kukula kwa uzimu kodabwitsa. Anamvetsetsa kuti ngati akufuna kupeza zambiri za chipatso cha Mzimu, zofuna zawo ndi chifuniro chawo munyengozo ziyenera kufa. Choncho zinthu zikachitika motsutsana ndi chifuniro chawo, ankakondwa kunena kuti tsopano anali ndi mwayi wochita chifuniro cha Mulungu m’malo mwa chawo. Izi zimatanthauza kuti anayenera kunena Ayi ku machitidwe awo a umunthu, ndipo zotsatira zake zinali zakuti silinalinso tchimo la mu m'khalidwe wawo limene linkalamulira machitidwe awo, koma Mulungu amatha kuwatsogolera kudzera m’Mawu Ake ndi Mzimu Woyera.

 Kukhulupirira kuti Mulungu ankagwira ntchito 

Ngakhale zinali choncho, amayi anga ananena kuti nthawi zina sankamva ngati akupita patsogolo pogonjetsa mkwiyo wawo. Koma kenako anagwiritsitsa mawu a Mulungu ku Afilipi 1:6, “Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.” Mulungu analonjeza kuti adzamaliza ntchito imene anayamba mwa iwo, ndipo ankadziwa kuti tsiku lidzafika limene adzakhala omasuka kotheratu ku mkwiyo woopsa umenewu.

Zotsatira zake zinali zakuti tonse timatha kuona mmene anasinthira. Kukhumudwa kwawo ndi nyengozo kunalowedwa m’malo ndi chimwemwe ndi kuleza mtima. Kusinthaku kunawapangitsa kukhala mayi wabwino kwambiri komanso kunawapangitsa kukhala wosangalala kwambiri. Palibenso chilichonse chimene chikanatha kusokonekera!

Mwachitsanzo, kale ankatikwiyira tikachita zinthu molakwika, ndipo ankalankhula mawu okhadzula. Patapita nthawi tinazindikira kuti akugonjetsa mkwiyo umenewu. Anangosiya kukwiya. Tsopano timawadziwa kuti ndi wofatsa, wokoma mtima, ndi woleza mtima. Vesi ili limandibwerera m’maganizo ndikaganizira za mayi amene ndikumudziwa lero:

 “Kufatsa kwanu kuzioneka pamaso pa anthu onse. Ambuye anu ali pafupi.” Afilipi 4:5.

Ndi mkazi amene tsopano amaonetsa kukoma mtima ndi ubwino, kuleza mtima ndi chimwemwe. Zipatso za Mzimu zimene timaziona m’moyo wawo zimapangitsa ena kulakalaka kwambiri kufika ku moyo womwewo.

Koma chipatso cha Mzimu Woyera ndi chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, kukoma mtima, ubwino, kukhulupirika, kufatsa ndi kudziretsa …” Agalatiya 5:22-23.

Ndikudziwa motsimikiza kuti kusintha kumene ndinaona mwa amayi anga pamene ndinkakula kunali chinthu chaumulungu kotheratu. Kuwonjezera apo, zimandilimbikitsa kuti inenso ndifike ku moyo umenewu, kuti moyo wanga ukopenso ena, monga momwe moyo wa amayi anga unachitira kwa ine.

Zikomo kwambiri, amayi okondedwa, chifukwa cha chitsanzo chimene mwakhala. Ana anu adzakhala okuthokozani mpaka kalekale chifukwa chotisonyeza kuti n’zotheka ndiponso n’kopindulitsa kusintha kwathunthu!

Positi iyi ikupezekanso ku

Nkhaniyi yachokera pa nkhani ya Carl Henry yomwe inasindikizidwa koyamba pa https://activechristianity.org/ ndipo yasinthidwa ndi chilolezo kuti igwiritsidwe ntchito pa tsamba lino.