Kodi tingatumikiredi bwanji Mulungu?

Kodi tingatumikiredi bwanji Mulungu?

Timawerenga zambiri zokhudza kukhala atumiki a Mulungu m’Baibulo. Koma kodi tingamutumikire bwanji kwenikweni?

9/19/20264 mphindi

Ndi Moyo wa Chikirisitu Wochitachita

Kodi tingatumikiredi bwanji Mulungu?

Mulungu anatipatsa malamulo Ake kuti atithandize

Kodi munthu n’kukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi ngakhale munthu wanzeru angamupindulire Iye? Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi Iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?” Yobu 22:2-3.

 “Inuyo mukachimwa, Iyeyo zimamukhudza motani?  Ngati machimo anu ndi wochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?  Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera m'dzanja lanu?  Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.” Yobu 35:6-8.

Kuchokera m’mavesi amenewa tikumvetsa kuti Mulungu satifuna ife, koma ife timamufuna Iye. Sakhudzidwa ndi uchimo wathu kapena ndi chilungamo chathu. Zimenezi zingakhudze anthu okha, anthu anzathu.

Timatumikira Mulungu tikamamvera malamulo amene Iye anatipatsa. Koma sanatipatse malamulo Ake chifukwa cha Iye mwini, kuti timuthandize tikawasunga. Ayi ndithu! Watipatsa malamulo Ake chifukwa cha ife, kuti atipatse nzeru, komanso kuti tikhale osangalala.

Kufunafuna ulemu ndi kusalungama

 Pali njira imodzi yokha imene tingatumikire Mulungu, ndipo ndiyo kukhala ndi moyo ndi kutumikira m’njira yoti Mulungu alandire ulemu ndi ulemerero. Tikatero timakhala olungama; apo ayi timachita zosalungama. “Iye wolankhula za iye yekha afuna ulemerero wake; koma iye wofuna ulemerero wa Iye amene adamtuma ali woona, ndipo mwa Iye mulibe chosalungama.” Yohane 7:18.

Ndinu osalungama ngati mumanena kuti, “Ambuye, Ambuye!” ndi kufunafuna ulemu wanu nokha. Pamenepo sizithandiza kuti mwachita zinthu zambiri zodabwitsa m’dzina la Yesu; mwadzitumikira nokha, osati Yesu. Yesu anafotokoza zimenezi momveka bwino pamene anati: “Ambiri adzati kwa Ine patsikulo, Ambuye, Ambuye, kodi sintikanenera m'dzina lanu ndi m'dzina lanunso tinkatulutsa ziwanda ndi kuchita zodabwitsa zambiri?  Pamenepo ndidzawauza momveka bwino kuti, Sindinakudziweni inu, Chokani kwa Ine, inu ochita zoipa!’” Mateyu 7:22-23.

Izi zingakhale zovuta kuzimvetsa. Kodi akanatha bwanji kuchita zinthu zazikulu chonchi m’dzina la Yesu, komabe Iye sanawadziwe? N’zosavuta kwambiri; zinali chifukwa chakuti anachita kusalungama uku: anatenga ulemu chifukwa cha zimene anachita. Ulemu ndi mphamvu ndi za Mulungu yekha (1 Timoteo 6:16). Ngati mutenga ulemu uliwonse umenewo nokha, ndinu wonyenga. Ndipo sizithandiza kunena kuti, “Ambuye, Ambuye!” kapena “Ulemerero wonse kwa Mulungu!”

 Paulo anali mtumiki wokhulupirika wa Ambuye. Anamva kuti zingakhale zochititsa manyazi kwa iye ngati Khristu sanalemekezedwe kudzera m’thupi lake. “Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pang'ono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa m'thupi langa kaya ndi m'moyo kapena mu imfa.” Afilipi 1:20. Sanapeze atumiki ambiri okhulupirika otere. Pamene analemba izi, anati anali ndi Timoteo yekha; ena onse ankangoganizira za iwo okha, osati zinthu zimene zinali zofunika kwa Yesu Khristu. Afilipi 2:19-23.

Ngati anthu akufuna kupeza ulemu chifukwa cha zimene amachita, zilibe kanthu kuti amakwaniritsa chiyani kapena amadzipereka bwanji; kaya amachita zimenezo pofuna kufalitsa uthenga wabwino kapena kupulumutsa miyoyo, amatumikira iwo eni ngati akufuna ulemu wawo mwa kuchita zimenezo. Pamenepo sasamala moona mtima. Mulungu anapanga Paulo kukhala mtumwi kuti atsogolere anthu pakati pa mitundu yonse kuti akhale omvera ku chikhulupiriro, ku ulemerero wa Yesu Khristu. Aroma 1:5. Akanagwira ntchito pofuna ulemu wake, sakanakhala wokhulupirika. Akanakhala wosalungama.

Tumikirani Mulungu – lemekezani Mulungu

Yesu ndi chitsanzo pofunafuna ulemu wa Mulungu, monga momwe Iye alili chitsanzo pa china chilichonse. Lingaliro Lake lokha linali kulemekeza Atate Wake. Pa nthawi za mavuto aakulu ndi kuvutika, pemphero Lake linali lakuti dzina la Atate Wake lilemekezedwe, osati kuti Iye apewe vutolo. “Moyo wanga ukuvutika tsopano, kodi ndidzanena chiyani? Ndinene kuti Atate pulumutseni ku nthawi ino? Ayi.  Chifukwa chimene Ine  ndinabwera pa nthawi iyi ndi chimenechi.  Atate lemekezani dzina lanu!” Yohane 12:27-28. Ngati ili ndi pemphero lathu pamene tili munyengo zovuta, nyengo yovutayo nayonso idzakhala yaulemerero kwa ife.

 Pamene Yesu anafotokoza ntchito Yake padziko lapansi, Iye ananena ndi mawu otsatirawa: “Ndakulemekezani padziko lapansi potsiriza ntchito imene munandipatsa kuti ndichite.” Yohane 17:4. Tikutumikira Mulungu ngati tili ndi maganizo omwewo pa chilichonse chimene timachita.

Positi iyi ikupezekanso ku

Nkhaniyi yachokera pa nkhani ya Sigurd Bratlie yomwe inayamba kuwonekera ndi mutu wakuti “Kutumikira Mulungu” mu magazini ya BCC ya “Skjulte Skatter” mu Januwale 1964. Yamasuliridwa kuchokera ku Norwegian ndipo yasinthidwa ndi chilolezo kuti igwiritsidwe ntchito pa tsamba lino.