Kodi mumakonda Yesu, ndipo mumakhulupirira kuti ndinu m'modzi mwa abwenzi Ake enieni? Uwu ndi ubale umene tiyenera kukhala nawo ndi Yesu ngati tikufuna kukhala naye muyaya.
Koma pali kusiyana kotani pakati pa kungokhulupirira Iye, ndi kukhala ndi ubale weniweni ndi Iye? Ubale umene Iye amakhala m'mitima mwathu, umene timafanana Naye kwambiri tsiku ndi tsiku?
“Ngati mundikonda Ine, sungani malamulo anga”
Yesu akunena m’buku la Yohane 14: “Ngati mundikonda Ine, sungani malamulo anga … Amene ali nawo malamulo anga, nawasunga, iyeyo ndiye amene andikonda Ine … Ngati wina andikonda, adzasunga mawu anga; ndipo Atate wanga adzamkonda, ndipo tidzabwera kwa iye, ndi kukhazikika naye.” Yohane 14:15,21,23 (CCL).
“Mwa ichi tidziwa kuti tili mwa Iye. Iye amene anena kuti akhala mwa Iye, ayenera iyeyo kuyendanso momwemo monga anayendera Iye.” 1 Yohane 2:5-6 (CCL).
Yesu watheketsa kuti tisunge malamulo amenewa ndi kukhala ofanana Naye tsiku ndi tsiku! Ndipo watipatsa Mzimu Woyera monga Mthandizi. Tikhoza kusunga malamulo Ake onse ponena kuti Ayi ku zofuna zathu ndipo osagonjera ku uchimo mwadala. Adzatipatsa mphamvu zonse ndi thandizo pa izi, ngati tidzipereka tokha kwa Iye.
Kuchita chifuniro cha Atate
“Si yense wakunena kwa Ine, Ambuye, Ambuye, adzalowa mu ufumu wakumwamba; koma iye amene achita chifuniro cha Atate wanga wakumwamba. Tsiku lija ambiri adzati kwa Ine, Ambuye, Ambuye, kodi sitinanenera m’dzina lanu, ndi kutulutsa ziwanda m’dzina lanu, ndi kuchita zozizwitsa zambiri m’dzina lanu? Ndipo pomwepo ndidzawauza iwo, Sindinakudziweni inu; chokani kwa Ine, inu ochita zoipa.” Mateyu 7:21-23 (CCL).
Ndikofunika kwambiri kusunga malamulo Ake; pamenepo Yesu alipo kwa ife pamene tipempha thandizo. Ngati tichita chifuniro chathu, ndi kuswa malamulo Ake, ndiye kuti chowonadi n’chakuti timadzikonda tokha, osati kukonda Yesu. “Iye amene anena, ndamdziwa Iye, ndipo sasunga malamulo ake, ali wabodza…” 1 Yohane 2:4 (CCL).
Powerenga za Yesu ndi mmene Iye anayendera pa nthawi yake padziko lapansi, tikhoza kuona kuti malamulo Ake ndi ati, chimene tiyenera kuchita kuti timutsate. Malamulo a Mulungu kwa ife m’nthawi yathu ali omveka bwino m’mawu Ake. Mwachitsanzo onani Mateyu 22:37-40 (CCL) pamene Yesu akuti: “‘Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse.’ Ili ndilo lamulo lalikulu ndi loyamba. Ndipo lachiwiri lofanana nalo ndi ili, ‘Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.’ Pa malamulo awiri awa pakhazikika lamulo lonse ndi aneneri.” Werenganinso Mateyu 5:28 ndi 1 Yohane 2:15.
Baibulo limanenanso kuti malamulo a Mulungu adzalembedwa m’mitima mwathu m’malo mwa mapale amiyala monga momwe zinalili nthawi Yesu asanabwere padziko lapansi. “Ili ndilo pangano limene ndidzapangana nawo pambuyo pa masiku amenewo, atero Ambuye; Ndidzaika malamulo anga m'mitima mwawo, ndi m'maganizo mwawo ndidzawalemba.“ Ahebri 10:16 (CCL). Tapatsidwa Mzimu Woyera monga Mthandizi m’nthawi yathu, kutiphunzitsa chifuniro cha Mulungu ndi kutikumbutsa mawu Ake. (Yohane 14:26, CCL).
Malonjezo kwa iwo amene asunga malamulo Ake
Monga momwe pali machenjezo omveka bwino kwa iwo amene amapempha thandizo kwa Yesu koma osasunga malamulo Ake, palinso malonjezo aakulu kwa iwo amene amamukonda Iye moona (iwo amene amasunga malamulo ake)! “Koma monga kwalembedwa: ‘Zimene diso silinazione, ndi khutu silinamve, ndipo sizinalowe mumtima mwa munthu, zinthu zimene Mulungu wawakonzera iwo amene amkonda Iye.’” 1 Akorinto 2:9 (CCL).
Pamene tiyamba kusunga malamulo Ake ndi kukhala ndi moyo m’mawu Ake, pang’onopang’ono timakhala ofanana ndi Yesu tsiku ndi tsiku. Pamenepo tidzakhala osangalala kwambiri ndi oyamikira malamulo Ake; amabweretsa mpumulo weniweni ndi chisangalalo chimene dziko lapansi silingatipatse.
“Ndikondwera kuchita chifuniro chanu, Mulungu wanga; inde, lamulo lanu lili mkati mwa mtima wanga.” Salimo 40:8 (CCL). Ngati tili nazo chonchi, ndiye kuti malamulo Ake sadzakhala ovuta kwa ife konse. “Pakuti ichi ndi chikondi cha Mulungu, kuti tisunge malamulo ake; ndipo malamulo ake sali olemetsa.” 1 Yohane 5:3 (CCL).
Tiyenera kuphunzira kusunga malamulo onse a Yesu ngati tikufuna kukhala naye limodzi kwamuyaya; ngati tikufuna kukhala osangalala ndi omasuka pakati pa zonse zomwe zimabwera m'njira yathu m'moyo wathu padziko lapansi.
Timadziwa m’mitima mwathu momwe tilili. Ngati sitinachite bwino, ndiye kuti tikhoza kupanga chisankho chatsopano chosinthira mmene tikukhalira ndi kukonda Yesu m’malo mwake; monga momwe Iye anatikondera ife poyamba.
“Pakuti zonse zili m'dziko, chilakolako cha thupi, ndi chilakolako cha maso, ndi kudzitama kwa moyo, sizichokera kwa Atate, koma ku dziko lapansi. Ndipo dziko lapansi lipita, ndi chilakolako chake; koma iye amene achita chifuniro cha Mulungu akhala ku nthawi zonse.” 1 Yohane 2:16-17 (CCL).